Home Uncategorized Mlembi wa mkulu wa chipani cha Malawi Congress Party MCP a Richard Chimwendo Banda apempha anthu m’boma la Ntchisi kuti adzavotere a Dr Chakwera pamasankho omwe aliko pa 16 September 2025.

Mlembi wa mkulu wa chipani cha Malawi Congress Party MCP a Richard Chimwendo Banda apempha anthu m’boma la Ntchisi kuti adzavotere a Dr Chakwera pamasankho omwe aliko pa 16 September 2025.

by Clary Simion
0 comments

Iwo anati boma la a Chakwera lachita zitukuko zambili monga kumanga misewu,kumanga zipinda zophuziliramo komanso kumanga nyumba za apolisi kungotchulako zochepa chabe.

Poyankha pa zomwe a Traditional Authority Kalumo anapempha a Chimwendo anati Boma layika kale ndalama zambili mu budget ya chaka cha 2025 kufika 2026 zomwe zithandize kuti amalawi asafe ndi njala komanso feteleza abwera ochuluka kuti anthu akalimire kudimba.

Iwo amalankhula izi pa msonkhano wa ndale omwe chipani cha Malawi Congress Party MCP chinachititsa pa Makanda primary school ground m’boma la Ntchisi komwenso ndikudera la olemekezeka a Ulemu Chilapondwa.

Olemba: Chifuniro Chikaphonya (13 April 2025)

NY FM mphanvu kwa mzika

You may also like

Leave a Comment

Dowa Community Radio is a community-based radio station established in 2020 to be used as a tool of communication in Dowa district and surrounding areas to facilitate issues of Education, gender-based violence, culture, child trafficking, Agriculture, Climate change and environment, transparency and accountability, sports, community self reliance, and many more.

Newsletter

Subscribe my Newsletter for new blog posts, tips & new photos. Let's stay updated!

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00