Home Uncategorized Tiyembekeze kukhala ndi chisankho cha mtendere, Mkulu wa NICE ku Ntchisi watelo.

Tiyembekeze kukhala ndi chisankho cha mtendere, Mkulu wa NICE ku Ntchisi watelo.

by Clary Simion
0 comments

Mkulu wa bungwe la National Initiative for Civic Education NICE wa m’boma la Ntchisi a Adam Disi ati bungwe lawo ndilokozeka kuphuzitsa anthu onse okhudzidwa za ubwino ochita ndale mwa bata.

Iwo anati ngati bungwe la NICE akhala akuchititsa misonkhano ndi adindo komanso anthu onse m’bomali pofuna kuwonetsetsa kuti tidzakhale ndi chisankho cha mtendere pa 16 September 2025.

“Ife tikhala tikuyenda mumisika komanso tikumana ndi adindo osiyanasiyana pofuna kufalitsa uthenga wakuti pasankhale ziwawa pa ndale” anatero a Disi.

Pogwilizana ndi a Disi mfumu yayikulu Kalumo ya m’bomali yati yayamba kale kukumana ndi mafumu kuwadziwitsa za udindo wawo pofuna kuti chisankho chikubwelachi chidzakhale cha Mtendere.

Iwo alankhula izi lero mu pologilamu yapandera yomwe bungwe la NICE linakoza pawailesi ya Ntchisi Youth FM ndipo mu programyi munalinso a Sub-Inspector Mzembe kuchokera ku polisi ya Ntchisi ndi a Mwawonanji Kachisuzi yemwe ndi mkhalapampando wa achinyamata m’boma la Ntchisi.

Olemba : Chifuniro Chikaphonya (27 March 2025)
NY FM mphanvu kwa mzika

You may also like

Leave a Comment

Dowa Community Radio is a community-based radio station established in 2020 to be used as a tool of communication in Dowa district and surrounding areas to facilitate issues of Education, gender-based violence, culture, child trafficking, Agriculture, Climate change and environment, transparency and accountability, sports, community self reliance, and many more.

Newsletter

Subscribe my Newsletter for new blog posts, tips & new photos. Let's stay updated!

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00