Tiyembekeze kukhala ndi chisankho cha mtendere, Mkulu wa NICE ku Ntchisi watelo.

Mkulu wa bungwe la National Initiative for Civic Education NICE wa m’boma la Ntchisi a Adam Disi ati bungwe lawo ndilokozeka kuphuzitsa anthu onse okhudzidwa za ubwino ochita ndale mwa bata.

Iwo anati ngati bungwe la NICE akhala akuchititsa misonkhano ndi adindo komanso anthu onse m’bomali pofuna kuwonetsetsa kuti tidzakhale ndi chisankho cha mtendere pa 16 September 2025.

“Ife tikhala tikuyenda mumisika komanso tikumana ndi adindo osiyanasiyana pofuna kufalitsa uthenga wakuti pasankhale ziwawa pa ndale” anatero a Disi.

Pogwilizana ndi a Disi mfumu yayikulu Kalumo ya m’bomali yati yayamba kale kukumana ndi mafumu kuwadziwitsa za udindo wawo pofuna kuti chisankho chikubwelachi chidzakhale cha Mtendere.

Iwo alankhula izi lero mu pologilamu yapandera yomwe bungwe la NICE linakoza pawailesi ya Ntchisi Youth FM ndipo mu programyi munalinso a Sub-Inspector Mzembe kuchokera ku polisi ya Ntchisi ndi a Mwawonanji Kachisuzi yemwe ndi mkhalapampando wa achinyamata m’boma la Ntchisi.

Olemba : Chifuniro Chikaphonya (27 March 2025)
NY FM mphanvu kwa mzika

Related posts

Bugwe la Muslim Association of Malawi (MAMU) linayitanitsa mkumano wa adindo osiyanasiyana ogwila ntchito zaboma komanso kudela kuphatikizapo achinyamata ndi cholinga chakambilana khani zauchembele wabwino komanso ubeleki.

Ntchisi Organization for Youth and Development (NOYD) in partnership with Save the Children International with funding from SIDA facilitated and supported Review Meeting on the Resolutions made during 2024 Ntchisi District Children’s Parliament Session. The meeting aimed at assessing the achievements by various duty bearers in the district. The meeting was conducted from 25th to 26th April, 2025 at Ntchisi Executive Lodge, Ntchisi.The duty bearers were the District Commissioner, 2 Senior Traditional Authorities, Malenga and Kalumo, District Council Chairperson and Heads of various sectors like Education, Forestry, Labour, Social Welfare as key respondents.During the meeting 20 Child Members of Parliament attended representing other Child Parliamentarians across the district.Major issues raised were Child Labour, Inadequate bursary support to needy students, unfriendly disability infrastructures in schools and Environment and Climate Change as a Child Rights issue with focus on depletion of trees for charcoal making.The house finally found that many issues from 2024 Child Parliament Resolutions were not solved by duty bearers. Therefore, the meeting agreed to table the unsolved issues in the 2025 Child Parliament Session.Ntchisi District Council